Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 166

Miyambi ya Patsokwe Musamaumirire mtunda wopanda madzi. -Osamakanirira pa zinthu zomwe zilibe phindu chifukwa zin- gangotitayira nthawi. Musamayese ndi masweswe, ndi dazi. -Mawuwa amenenedwa munthu akamatsimikizira kuti zimene akunena ndi zoona zenizeni. Musandiike chibanzi pakamwa. -Musandiletse kunena zomwe ndikufuna kunena. Musandiike dzungu pakamwa. -Musandiletse kunena zomwe ndikufuna kunena. Musandipatse masamba chifukwa pali kapado. -Mwambiwu umanena za kukhutira ndi zabwino zimene mun- thu ali nazo. Ku Africa kuno pamene munthu wadyera nyama ndiye kuti paterela. Choncho, amafuna kuiwalako kudya masamba akakhala kuti wapeza nyama. Musandiyangire nkhata pakamwa. -Musandiletse kunena zomwe ndikufuna kunena. Musandiyese chulu cha ndiwo chokwera ndi nthekwe m’chi- uno. -Si bwino kuyesa munthu wina ngati wopusa kuti az- ingokuthandiza nthawi zonse. Tiziyamikira zimene ena amati- chitira. Musawongole mbewa yopondaponda. -Ukadziwa kuti walakwa ndi bwino kungopepesa osachita makani. Musayese ndi masweswe, limeneli ndi dazi. -Si bwino kumanyozera zinthu anthu ena akamanena. Mutu ukakula sulewa nkhonya. -Munthu ukakhala wamkulu mavuto onse amafikira kwa iwe. 165