Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 164

Miyambi ya Patsokwe Munthu salakwira mtengo. -Kulikonse anthu amalakwirana ndipo palibe amene salakwa. Choncho, zikachitika ndi bwino tizikhululukirana. Munthu samenyana ndi maliro. -Tisamalimbane ndi munthu yemwe ali wofooka kwambiri. Munthu sangadziteme mphini kumbuyo. -Timafunika anthu ena kuti atithandize pa zinthu zina. Munthu satola kanthu ndi chala chimodzi. -Kugwirizana komanso kuthandizana n’kofunika kwambiri. Munthu wadyera adanka ndi mvula ya mawawa. -Munthu wokonda kuchita chiwerewere amafa nsanga potenga matenda. Munthu wamagwiragwira samera tsitsi loyera. -Munthu wamakhalidwe oipa sakalamba. Munthu waphuma adapsa paphewa. -Kupupuluma kumawononga zinthu. Ndi bwino kumafatsa. Munthu wokhulupirika anaipitsira m’basi. -Nthawi zina kukhala wokhulupirika kwambiri kumabweretsa mavuto kapena kungachititse kuti munthu achite zochititsa manyazi. Munthu wolemera safa ndi chuma. -Tiyenera kukhala ndi chuma kuti chitithandize pamoyo wathu. Munthu wongodutsa amene amalowerera mkangano womwe si wake n’kukwiya nawo, ali ngati munthu wogwira makutu a galu. -Osamalowerera nkhani imene sikutikhudza. Munthu amene wagwira makutu a galu amafunika kusamala chifukwa akangowasiya makutuwo, galuyo amatha kumuluma. 163