Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 163

Miyambi ya Patsokwe Mumphasa yongoima mumabisala zoluma zambiri. -Munthu amene wangokhala chete, timuope. Mumphuno imodzi simulowa zala ziwiri. -Umafunika kuchita chinthu chimodzi kaye. Ukaphatikiza zin- gapo umatha kuwononga zonse. Mungatero, mwaperekeza mwana wolima. -Mwambiwu umanenedwa anthu akamadandaula kuti munthu yemwe amamudalira pamudzi kapena pakhomo wachoka. Munthu akamafuna kufa, amayamba ndi makutu kutsekeka. -Kusamvera kumapezetsa munthu mavuto aakulu monga imfa. Munthu akatsala pang’ono kufa, amayamba ndi makutu kufa. -Kusamvera kumapezetsa munthu mavuto aakulu monga imfa. Munthu amene sakhululukira mnzake amakhala akuphwas- ura mlatho woti aolokerepo yekha. -Aliyense amalakwitsa, ndiye ngati munthu sakhululukira anzake, anzakewonso samukhululukira. Ndi bwino mnzathu akatilakwira tizimukhululukira kuti tsiku lina nafenso tikadzala- kwitsa adzatikhululukire. Munthu azilimba ngati mthiko, chipande chilira madzi. -Tisamangodalira chithandizo chochokera kwa anthu ena ngati chipande, tizilimba ngati mthiko n’kumadzithandiza tokha. Munthu ndi Galu, Galu ndi munthu. -Nthawi zina Galu amachita zabwino kuposa munthu kapenan- so zabwino zomwe zimafanana ndi zochita za anthu ena. Anthu ena kuwachitira zabwino sayamika, pomwe Galu ama- kugwedezera mchira posonyeza kuyamikira. Munthu sakula pa kamwini, amakula pa kake. -Munthu aliyense sakhala ndi ulamuliro pa chinthu chamwini koma chake. Tiyenera kugwira ntchito kuti tipeze zathu. 162