Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 162

Miyambi ya Patsokwe Mtunkhatunkha udayatsa lipande. -Munthu ukamakhuthulakhuthula mphale, ina imataika. Nafen- so tiyenera kukhala anthu okhazikika m’malo momati apa tag- wira apa tagwira, tikhoza kugwira posagwira kapena kuwonon- ga zinthu. Lipande ndi mphale. Mudzi umalimba ndi anyamata. -Dziko lililonse liyenera kusamalira ndi kunyadira achinyamata chifukwa ndi amene adzakhale atsogoleri amawa. Mukanakhala mbewu, tikadangokazinga. -Mawuwa amanenedwa akamafotokoza za anthu ovuta kapena ana ovuta. Anthu ena akakwiya amanena mawuwa potanthauza kuti anthuwo ndi amphulupulu omwe sangawasunge pakhomo. Mukhoza kusinja chitsiru mumtondo, koma uchitsiru wakewo sungamuchoke. -N’zovuta kuthandiza munthu wopusa. Mulereni ayiwale kwawo. -Mwana wamasiye kapena wa ena amafunika kumulera bwino kuti aiwale kwawo kapena mavuto amene akukumana nawo. Mulimbalimba goli lili m’khosi. -Munthu ukagwidwa ndi mlandu, ngakhale udziteteze bwanji zimakhala zopanda phindu chifukwa umboni wonse uma- kutsutsa. Mulungu amapatsa wolimbika. -Tiyenera kumadzithandiza tokha ngati tikufuna kuti Mulungu atithandize. Mulungu amapatsa wopirira. -Tiyenera kumadzithandiza tokha ngati tikufuna kuti Mulungu atithandize. 161