Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 161

Miyambi ya Patsokwe Mtima wake waika pa mfuti. -Kuchita mwano kapena kukula mtima chifukwa choti uli ndi podalira. Mtima walasa phaso. -Mwambiwu umanena za munthu yemwe wakumbukira kwawo. Ungatanthauzenso kuti ndapeza chokhumba cha mtima wanga. Mtima wamnzako ndi m’thumba, sudziwa chomwe chilimo. -Zomwe wina akuganiza n’zovuta kuzidziwa. Mtima wamnzako ndi tsidya lina. -Za mumtima wa munthu wina sungazidziwe. Mtolo waukulu suchiza njala. -Ndibwino kumayamikira zimene tili nazo ngakhale zochepa. Mtsinje umalimba ndi miyala. -Kudya n’kumene kumathandiza munthu kuti akhale wam- phamvu. Mtsinje wa Tinkanena udathera mu Siizi. -Mawu a akulu amakumbukiridwa pakapita nthawi ndiponso pamene zomwe amanena zachitikadi. Munthu akakhala wos- amva akamalangizidwa zotsatira zake amakumana ndi mavuto. Mtsinje wopanda miyala susunga madzi. -Miyala ndi imene imathandiza kuti madzi azisungika mumtsinje. Chimodzimodzinso m’mudzi, mfumu imafuna an- thu oithandiza pa zinthu zambiri. Mtsuko sulowa m’chikho, koma chikho ndicho cholowa mumtsuko. -Munthu waudindo ndi amene amalandira ulemu kuchokera kwa otsika, koma iyeyo sapereka ulemu kwa anthuwo. 160