Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 159

Miyambi ya Patsokwe Msuma sudyera pomwepo. -Msuma ndi chakudya kapena zinthu zomwe tapatsidwa popemphetsa panthawi ya njala. Ndi bwino kukumbukira banja lako chifukwa nawonso akufuna kudya. Tiziganizira anzathu ovutika. Mtakataka kunsengwa, kumunda kumlaka. -Pali anthu ena omwe amajijirika pakakhala zakudya, kun- sengwa basi (kale anthu ankapakulira chakudya munsegwa, mbale zisanabwere). Koma akauzidwa kuti akalime amakana. Mtanga umakoma ndi kusomekera. -Pochita zinthu pamafunika kuchita khama kuti zimene tikufuna zitheke kaya ndi kusukulu kapena pantchito. Mtaya makoko saiwala, amaiwala ndi m’dya nyemba. -Munthu ukakhala pamavuto suiwala wina akakuchitira zoipa, koma wochita zoipazo amaiwala. Mtedza woola umalavulitsa zonse. -Kulakwa kwa munthu m’modzi kumaipitsa mbiri ya banja lonse kapenanso dziko. Mtengo suphuka masamba usanagwetse akale. -Kusintha kwenikweni kumabwera ngati munthu wasiya zimene amachita poyamba. Mtengo umagwera kumene waweramira. -Nthawi zambiri ana amachita zimene amaona makolo awo aku- chita. Ungatanthauzenso kuti munthu akakhala wakhalidwe loipa amadzafa ndi khalidwe lakelo. N’kovuta munthu kuleka chizolowezi chake. Mtengo usamakome pokwera pokha. -Si bwino kumakonda anthu tikamafuna chinachake kuchokera 158