Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 158

Miyambi ya Patsokwe Mseka pamwamba, m’kati mwa mtima muli zina. -Kuonetsa chisangalalo pamaso koma mumtima muli chiwem- bu. Msika ndi wekha. -Kuti zikuyendere umafunika kuchita khama. Msipu suyenda, imayenda ndi nyama. -Ngati munthu akusowa chinthu ayenera kupita kukachifunafu- na chifukwa sichingamupeze pamene wakhalapo. Msipu wamera m’khola. -Kuchita mwayi kuti zimene umafuna zachitika mmene umafu- nira. Kupeza mwayi waukulu. Msipu wobiriwira udapha mbuzi. -Mbuzi itapeza msipu wobiriwira inkangodyabe mpaka ina- phulika mimba. Tisamakomedwe ndi zinthu ngakhale zitakhala zokoma bwanji chifukwa pamapeto pake tikhoza kupeza mavuto. Msirikali wa atate (imfa) ndiye amachotsa chimwemwe. -Imfa ikamachitika kawirikawiri pakhomo anthu sakhala osan- galala. Msonjosonjo andautsa amene ali chete. -Msonjosonjo ndi kulozana zala. Nthawi zambiri anthu aka- maloza anzawo chala amapangitsa kuti amene anali chete akwiye. Ungatanthauzenso kuti nthawi zina anthu apachibale akamadana zimapangitsa kuti anthu adera alowererepo. Msonkhasonkha unang’amba thumba. -Munthu akamangotolera pang’onopang’ono osasiya, zima- chuluka kwambiri ndipo kenako zmawonongeka. Nthawi zina ndi bwino kuchita zinthu mosathamanga komanso ndi bwino kulimbikira kuti zomwe ukufuna zitheke. 157