Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 157

Miyambi ya Patsokwe ndi akuluakulu. Zikakuvuta anthu omwewa ndi amene amaku- thandiza. Mphwayi ndi tsoka, ulesi ndi minyama. -Munthu wamphwayi sangapeze zimene akufuna. Tizichita kha- ma pazinthu. Mphwayi ndi tsoka. -Munthu wamphwayi kapena waulesi satukuka ndipo ama- kumana ndi mavuto adzaoneni. Mphwayi zilibe mtolo. -Ulesi umabweretsa umphawi. Tiyenera kumagwira ntchito kuti tipeze zimene tikufuna. Mpingu saloza ndi chala. -Mpingu ndi munthu amene amakhala ndi ulamuliro wovo- mereza zinthu zofunika. Ngati utamuloza ndi chala ndi mwano. Mwambiwu umatanthazua kuti si bwino kumanyoza anthu om- we angatithandize. Mpotepote m’poyamba, potsiriza n’chingwe. -Zinthu zimaoneka zonyozeka poyamba koma zikakula zimatha kupanga zazikulu. Mwachitsanzo, kuba zinthu zing’onoz- ing’ono kukhoza kudzatibweretsera mavuto aakulu. Mpsalazingo wamukho wapamwala. -Mawuwa amanena za munthu amene amakhala wochenjera kwambiri pozemba ntchito kapena mlandu chifukwa chodziwa kuyankhula. Mseche udaombola mbiya. -Aliyense ndi wofunika pambali inayake. Ngakhale ena azioneka onyozeka tiyenera kumawalemekeza chifukwa akhoza kudzatithandiza. 156