Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 155

Miyambi ya Patsokwe n’kupita kukazikhuthura kwina. Amachitanso chimodzimodzi ndi zimene wamva kumeneko. Mphamba ikasowa Nkhukhu imatola udzu. -Ukakhala pamavuto susankha, kunyada umakusiya kaye apo, n’kuyesetsa kuchita chilichonse kuti uthandizike. Mphamvu za Ng’ona zili kumchira. -Anthu audindo amakhala ndi mphamvu chifukwa cha anthu omwe akuwalamulira. Choncho, ayenera kumalemekeza an- thuwo. Mphamvu zimaphetsa. -Kudzitukumula kumabweretsa mavuto. Ukakhala ndi mphamvu kumalemekeza ena chifukwa tsiku lina ungadza- kumane ndi wina wamphamvu kuposa iweyo n’kukumenya. Mphawi dziko alidyera ku uchi. -Ngakhale munthu wosauka, anthu ena amamuitana kuphwan- do ndipo amadya nawo zabwino. Kuthandizana n’kofunika. Mphawi nayenso ndi mzimu, musamunyoze. -Munthu aliyense ayenera kulemekezedwa ngakhale wosauka. Mphechepeche mwa Njovu sapitamo kawiri. -Ngati tapulumuka pa zoopsa, monga kwa Ng’ona padziwe, si chanzeru kubwereranso chifukwa mapeto ake tikhoza kugwid- wa n’kulephera kudzipulumutsa. Mphemvu m’dyera kum’thiko. -Mawuwa amanena za munthu wosauka yemwe amapeza zin- thu movutikira monga chakudya ndi zina. Mphenzi siimenya mtengo kawiri. -Pali zinthu zina zomwe zimachitika kamodzi kokha pamoyo wa munthu. Choncho ndi bwino kumagwiritsa ntchito mwayi umene tapeza. 154