Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 153

Miyambi ya Patsokwe Moyo kunyenga. -Munthu ukakhala ndi thanzi labwino umakhumba utachita zambirimbiri komanso umatha kunyoza abale ako kuiwala kuti tsiku lina udzadwala. Moyo ndi mpamba, usamalireni. -Kuti munthu achite chilichonse amafunika kukhala ndi moyo. Moyo saika pachiswe. -Tiyenera kupewa kuchita zinthu zomwe zingaike moyo wathu pangozi. Moyo samanga ndi njerwa. -Mwambi wosonyeza kuti umafunika kudya kuti ukhale ndi thanzi. Moyo uli ngati anyezi, timausenda tikulira. -Moyo ndi wovuta kwambiri. Masiku ambiri amatha munthu akuvutika. Moyo uli ngati moto, umafunika kusonkhezera. -Kuti zikuyendere umafunika kumasamalira moyo wako. Moyo wanga ndi kambiya, ndisunga ndekha. -Palibe munthu angakusamalire moyo wako koposa mwini wakewe. Moyo wanga ndi mbiya, ndisunga ndekha. -Munthu aliyense amasamalira moyo wake, choncho zikakuvuta suyenera kuloza munthu wina chala chifukwa udindo wosankha zochita pamoyo wako ulinso m’manja mwako. Moyo wathombozi wouma kumodzi. -Thombozi ndi mtengo womwe umauma mbali imodzi n’kukha- la moyo mbali imodzi koma suferatu. Mawuwa amatanthauza kuti ngakhale tili moyo, koma tikukumana ndi mavuto ambiri. 152