Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 152

Miyambi ya Patsokwe Mnzako ali pomwe (mnzako akakhala pafupi). -Mwambiwu umanena za munthu amene amaoneka ngati mnza- ko akakhala pafupi, koma akangokhala kumbali amayamba ku- kunena miseche. Mnzako si amene umadya naye n’kukhuta, koma amene amati zikavuta amabwera n’kudzakuthandiza. -Mnzako weniweni amaonekera pamavuto. Monga mphuno, maso amatakataka. -Tisamachite zinthu modzionetsera. Osamasonyeza anthu kuti ifeyo ndiye abwino kwambiri kuposa ena. Moto umapita kwatsala tchire. -Zikagwera ena, dziwa kuti watsala ndi iwe. Ndi bwino ku- mathandizana kuti nawenso zikakuvuta adzakugwire mkono. Moto wapathupi sakuuza ndi mnzako. -Vuto limene ukukumana nalo umalidziwa wekha, suchita kudikira kuti ena akuuze. Moto wopanda masekera umavuta kuyaka. -N’kovuta kuweruza mlandu popanda mboni. Mowa m’chimera. -Pochita zinthu pamafunika luso logwiritsa ntchito zinthu zo- funika kuti zinthu ziyende bwino. Mowa n’kumwera pamodzi. -Kuchitira zinthu limodzi n’kumene kungachititse kuti anthu asangalale kwambiri. Mowa n’kumwerana. -Kuti chibale chilimbe pamafunika kuyenderana komanso kuthandizana. 151