Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 149

Miyambi ya Patsokwe Mleleni bwino aiwale kwawo. -Pakhomo pakakhala akamwini kapena alendo timafunika ku- wasamalira bwino kuti asamadandaule n’kukumbukira kwawo. Mleme anangowola, sanaike maliro. -Mleme umakhala ngati zinthu ziwiri, khoswe komanso mbalame. Mleme utadwala unapita kwa mbalame ndipo zinaka- na kumulandira. Kenako unapita kwa makoswe ndipo nawonso anamukana. Mlemewo utafa palibe anaika maliro ake moti anangowolera pamtunda. Munthu wopanda anzake enieni amasowa omuthandiza. Mlendo ndi amene amadza ndi kalumo kakuthwa. -Mpofunika kumamva maganizo a alendo chifukwa mfundo zawo zikhoza kukhala zothandiza kwambiri. Mlendo akhoza kuthandiza pa vuto limene eni mudzi ali nalo. Mlendo ndi mame, sachedwa kulakatika. -Tisamachite nkhanza ndi alendo chifukwa sakhalitsa. Komanso umbombo umaonongetsa zambiri. Nkhani yake imanena kuti, kalekale panali mayi wina dzina lake Nasiketi. Nasiketi anali kudziwika kwambiri chifukwa cha umbombo. Tsiku lina anavuula mphale, ndipo atasinja ufa anaganiza kuti ndiwo zimene adyere nsima tsikulo zikhale nyama. Anasinjadi ufa wosalala bwino ndiponso anapezadi nyama yonona bwino imene anakagula pamudzi woyandikana ndi mudzi wawo. Pa nthawiyi Nasiketi anali asanataye matsukwa a mphale ija. Akumaliza kuphika nsima anamva panja munthu wina akuodi- ra. Poonetsetsa anaona kuti ndi mlendo amene sanali ku- muyembekezera. Apa nzeru zinamuthera Nasiketi. 148