Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 148

Miyambi ya Patsokwe Mkwita umodzi sulira m’mwendo. -Mkwita ndi chibangiri cha m’mwendo. Chikakhala chokha sichimalira. Zinthu zimayenda bwino kwambiri pakakhala an- thu ambiri. Mudzi umatchuka chifukwa cha zochita za anthu onse. Mlamumwako ndi Likongwe, akalowa mphanga koma ku- mutsekera ndi masamba. -Ukamuthandiza mnzako amene ali pamavuto ndiye kuti wamutsekera ndi masamba. Koma ukakana kumuthandiza ndiye kuti wamutsekera ndi mwala. Ena akatilakwira tiz- iwakhululukira. Mlandu sagula ndi chipanda cha mowa. -Si bwino kuweruza mlandu mokondera chifukwa choti wina watipatsa ziphuphu. Mlandu sugwera pamtengo. -Kulikonse anthu amalakwirana ndipo palibe amene salakwa. Choncho zikachitika ndi bwino tizikhululukirana. Mlandu suwola. -Ngakhale munthu atathawira kutali, mlandu wake amadzau- peza patapita zaka zambiri. Munthu akapalamula amakumana ndi zotsatira za zimene wachita kaya afune asafune. Mlandu uli m’kamwa. -Kuyankhula mosasamala kukhoza kutibweretsera mavuto. Mpofunika kumayamba taganiza kaye tisanayankhule. Tisakha- le a zikachitika mumvera kwa ife. Mlatho wathyoka, tsopano tiwoloka bwanji? -Mawuwa amatanthauza kuti gwero la chithandizo chathu laphwera, ndiye tikhala moyo bwanji? 147