Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 144

Miyambi ya Patsokwe zimene sizinachitike. Mimba njosadzitamira. -Si bwino kumadzitama chifukwa cha zinthu zomwe sizinachi- tike. Mwachitsanzo, mayi akakhala ndi pakati, sayenera kud- zitama mpaka atabereka. Mimba simapha namwino. -Namwino amangothandiza munthu kuti abereke. Ngakhale zitavuta bwanji, sangafe chifukwa cha mimba ya munthu wina. Amangofunika kuthandiza munthuyo basi. Chimodzimodzi pamlandu, ngati tafunsidwa, tiyenera kusachita mantha po- longosola zimene tikudziwa chifukwa mimba si yathu. Minga ikabaya, zula. -Ukakumana ndi mavuto ndi bwino kupeza njira yothetsera mavutowo. Minga ya pansana amakuzula ndi mnzako. -Pali zinthu zina zomwe sitingakwanitse tokha. Timafunika kuthandizidwa ndi ena. Miphika yaphulana. -Nthawi zambiri anthu okondana amadziwa zimene mnzawo akusowa. Kuthandizana n’kofunika. Misala si chamba chokha. -Pali zinthu zambiri zimene zingachititse kuti munthu akhale mwanjira inayake. Mwachitsanzo, munthu akhoza kudwala misala chifukwa cha matenda osati kusuta chamba. Miseche ilinda mwini. -Anthu akamanena za ena amafunika kusamala chifukwa akho- za kuwapezerera n’kumva zonse. Mitengo yoyandikana imaperesana. -Anthu akakhala pamodzi salephera kuyambana. 143