Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 143

Miyambi ya Patsokwe umakumana ndi mavuto ndi iweyo. Mfumu ndi nkhuti. -Munthu wamkulu kapena mfumu imadziwa zinthu zambiri zomwe sangaziulule wambawamba. Mfumu sidyera kuwiri. -Mfumu poweruza nkhani siyenera kukondera. Komanso si bwino kudikira kuti ena atichitire zabwino chifukwa choti ama- tidziwa, chifukwa akadzachoka tidzasowa kulowera. Mfumu sikoma kuwiri. -Mfumu poweruza nkhani siyenera kukondera. Komanso si bwino kudikira kuti ena atichitire zabwino chifukwa choti ama- tidziwa, chifukwa akadzachoka tidzasowa kulowera. Mfumu yandewu simanga mudzi. -Atsogoleri olongolola kapena okonda ndewu amapweteketsa anthu awo. Anthu akaona kuti mtsogoleri wawo ndi woipa ama- samuka pamudzi ndipo mudzi umapasuka. Mfuti yolasa woombera. -Nthawi zina zinthu zako zomwe, monga agalu ndi zina ndi zimene zimakupweteka. Mimba imodzi siibala nkhoswe. -Anthu apachibale ayenera kumakondana, chifukwa pamawa pamadzabwera zinthu zomwe ungadzafune kuti abale ako aku- thandize. Kuchulukana n’kofunika. Mimba ndi mtengakako, phewa ndi mtengakaeni. -Munthu ukakhala ndi chuma umafunika kumachidya, apo ayi amadzachichecheta ndi ena. Mimba ndi yanji? -Mayi akakhala ndi pathupi sitimadziwa kuti mwana amene adzabadwe adzakhala wotani. Si bwino kumawerengera zinthu 142