Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 142

Miyambi ya Patsokwe Mfiti Kuliritsa. -Munthu amene amalira kwambiri pamaliro ndi amene nthawi zina amakhala kuti wapha munthuyo. Mfiti yaikazi kulimba moyo. -Anthu amene amakhulupirira za ufiti amati mfiti yaikazi ndi imene siimva chisoni popha munthu. Mfiti yaikazi kuuma mtima. -Anthu amene amakhulupirira za ufiti amati mfiti yaikazi ndi imene siimva chisoni popha munthu. Mfiti zimadziwana. -Anthu okonda zofanana kaya zabwino kapena zoipa amadzi- wana. Mfulumira adameza nsima yamoto. -Tisamafulumire kuchita kapena kunena kanthu chifukwa chotengeka. Chifukwa tsiku lina tikhoza kudzanena kapena ku- chita chinthu chomwe chingadzatibweretsere mavuto. Mfulumira anadya gaga. -Kuchita zinthu mofulumira kwambiri kumapangitsa kuti mun- thu apeze mavuto kapena awononge zabwino zonse. Mfulumira sachedwa kugwa m’mbuna. -Kufulumira kapena kupupuluma kumagwetsera munthu m’mavuto. Mfumu n’kudzala. -Amfumu pamudzi kapena pantchito amakhala ngati kudzala chifukwa nkhani zonse zimakathera kwa iwo. Mfumu ndi mbatata, ukaongola wathyola. -Nthawi zambiri anthu omwe ndi otchuka kapena audindo waukulu amavuta kuwalangiza. Ukalimbana nawo 141