Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 141

Miyambi ya Patsokwe zinthu mosamala kuti tisapalamule. Mchenga woyera unathetsa madondwe. -Pali zinthu zina zomwe zimaoneka zabwino, koma pambuyo pake zimabweretsa mavuto aakulu. Mchepera wa Kalulu, mtima ndi phiri. -Nthawi zina anthu onyozeka kapena ovutika amakhumba ziku- luzikulu. Mdima umasaka. -Pamene walakwira makolo masana, umatha kuthawa. Koma kukada umapitanso kwa makolo ako n’kukalangidwa. Cholakwa sichithawika, nthawi imafika ndipo munthu ama- landira chilango cha zimene wachita. Mdima wa dzinja udakwatitsa mkazi wonyansa. -Zinthu zina zikamachitika zimaoneka ngati tsoka, koma nthawi zina zimabweretsa mwayi. Mwachitsanzo, mkazi wonyansa adakwatiwa chifukwa cha mdima wa dzinja. Mdima wamadzulo umathyola mwendo. -Tisamayende ndi anthu oipa chifukwa akhoza kutipaka mavuto. Mesewera sachedwa kubala ndewu. -Ukaona kuti macheza kapena masewera akulowera kwina- kwake koipa, ndi bwino kungochokapo chifukwa nthawi zina masewera abwinobwino kapena macheza amatha kusintha n’ku- khala ndewu ya mtima bii. Meta mpala opanda madzi. -Mawuwa amatanthauza kuchenjeretsa munthu kotheratu. Mfiti idzafanso. -Munthu ngakhale woipa bwanji amafabe. 140