Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 140

Miyambi ya Patsokwe Mbombo ndi mwala, mtengo umataya mayani. -Mwala sutaya kanthu. Koma mitengo imataya masamba. Mwambiwu umanena za munthu womana, yemwe safuna kuga- wira ena zinthu. Munthu wotero amangokhala ngati mwala. Mbumba n’kudyetsa. -Munthu ukakhala ndi ana kapena achibale umafunika ku- mawasamalira. Mbumba ndi anthu onse. -Tiyenera kumasamalira achibale onse mosasankha. Mbuto ya Kalulu idakula ndi tadzaoneni. -Mbuto kapena kuti malo okhala Kalulu amakhala aang’ono. Anthu atabwera kuti adzawaone, inakula chifukwa chopondaponda. Zinthu zazing’ono zimakula zik- amanenedwanenedwa chifukwa anthu amawonjezerapo bodza. Mbuzi ikacheuka yasiya mwana. -Tiyenera kumachita zinthu tikakakhala ndi zifukwa zomveka zochitira zinthuzo monga kujomba kuntchito, kusiya ntchito ko- manso zina. Mbuzi ikalawa zamchere sisiya. -Mbuzi ikalawa zinthu zokoma sisiya, imavuta koopsa. Chimodzimodzi ndi munthu amene wayamba khalidwe li- nalake, zimamuvuta kuti asiye. Amakhala ngati walawa zam- chere. Mbuzi ndi mkota. -Akuluakulu ndi ofunika pamudzi chifukwa amakhala aona zambiri pa moyo wawo. Ana amatengera zimene makolo awo amachita. Mbuzi ya gudu imafikira kumunsi. -Khalidwe loipa limachititsa kuti munthu alangidwe. Tizichita 139