Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 139

Miyambi ya Patsokwe anakakubweretsera imfa. Mbeta silola tsiku limodzi. -Sungafunsire mbeta n’kukulola koyamba. Tiyenera kukhalabe opirira ngati tikufuna kupeza zabwino. Mbewa yamanyazi inafera kuuna. -Mbewa ina sinafune kutuluka kuuna kuthawa utsi chifukwa cha manyazi ndipo inafera komweko. Tisamachite manyazi ndi anthu ena pakakhala zofunikira kuchita. Mbewa zikachuluka siziika masa. -Pa ntchito pakachuluka anthu, ntchitoyo siyenda. Mbewa zikachuluka sizitsekera. -Anthu akachuluka ntchito siyenda bwino. Aliyense aman- gosiyira mnzake. Mbewa zikatha amanona ndi aswiswiri. -Zinthu zabwino zikatha, zotsikirapo ndi zimene zimakhala zo- funika. Mbiri ndi ng’oma. -Mbiri imafalikira mwansanga kwambiri ngati ng’oma. Mbiri ya mnzako saimira pachulu. -Osamayalutsa mnzako ponena zimene amalakwitsa kwa ali- yense. Mbiya ikasweka siibwereranso, ndikafa ndafa ndatha. -Chinthu chikaonongeka chimavuta kuchibwezereretsa, monga munthu akafa wafa basi. Mbiya ikasweka siiwumbikanso. -Zinthu zina zikachitika, zachitika zatha. Sizingabwererenso ngati kale. 138