Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 136

Miyambi ya Patsokwe monena kuti mawu achinsinsi kapena mawu ena omwe anthu amanena kuseri, mwina kujeda munthu. Mawu amakoma kuti naye mdzakazi azikondwa. -Mawu okoma amasangalatsa aliyense. Tiyenera kukhala osama- la ndi zomwe timanena kuti tisakhumudwitse ena. Mawu mpoyamba, otsiriza m’mang’ombe. -Ndi bwino munthu kusamala mawu oyamba omwe ukufuna kuyankhula chifukwa ndi amene anthu omvetsera amaw- erengera kuti ndi zomwe wanena. Mawu ndi mphepo, sungawatchere msampha. -Tifune tisafune mawu ayenera kupita kulikonse. Mawu ndi ng’oma. -Tizichenjera ndi zimene timanena chifukwa tikayankhula sabwerakonso. Mawu ndi oyamba, otsiriza ndi mang’ombe. -Pa nkhani, mawu oyamba ndiye amakhala nkhani yeniyeni, ob- wera pambuyo pake amangokhala mang’ombe. Mawu ngotsogoza (ndi oyamba). -Munthu akalephera kunena zoona pamene wafunsidwa ndiye kuti ndi wolakwa. Tiyenera kumayamba kaye taganiza bwino ti- sanayankhule. Mawu okoma anatulutsa Ng’azi kumphako. -Anthu ena akafuna kuchitira ena zoipa kapena akamafuna ku- wabera amayankhula zosyasyalika, zokokomeza kuti apusitse munthuyo. Tiyenera kuchenjera ndi anthu amenewa. Mawu okoma ndi kamba, oipa ndi ndulu. -Mawu abwino amabweretsa mtendere, oipa amayambitsa nde- wu, mikangano komanso nkhondo. 135