Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 133

Miyambi ya Patsokwe amene sakhutira ndi zimene ali nazo. Maso amangofunabe kuti aone zina zatsopano. Maso samangira mpanda. -Maso akhoza kuona chilichonse, kaya ndi chabwino kapena choipa. Mawuwa amanenedwa ngati wina akunena kuti waona zinazake zoipa, ndiye potsutsa winayo amati maso alibe mpan- da. Matako saleka kuperesana. -Pamene pali anthu sipalephera kukangana kapena kusemphana chichewa. Matako sangatsogole ngakhale atafunitsitsa bwanji. -Matako amakhala kumbuyo basi, akhoza kufuna kutsogola ko- ma kwawo n’kumbuyo. Si bwino kumayesa kuchita zinthu zom- we sizingatheke. Matama a Kambuzi. -Makani opanda ntchito kapena ongofuna pofera. Matenda amabwera pagalimoto koma amachoka wapansi. -Matenda amabwera kamodzin’kamodzi koma amachedwa kuti achoke. Matenda bisani, maliro tidzamva. -Munthu sungathe kubisa zimene zikuchitika pamoyo wako chifukwa tsiku lina zidzamveka. Ndi bwino kuuza ena mavuto athu kuti atithandize. Osamabisa zinthu zimene simungakwanitse kuzibisa. Matukutuku a pida. -Mawu amenewa amanenedwa kwa anthu omwe ndi opanda mphamvu koma n’kumachita makani kuti akhoza kulimbana ndi adzitho. 132