Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 130
Miyambi ya Patsokwe
zazikulu kwambiri zimatha kutha.
Masiku amatha n’kugona.
-Tikamayembekezera chinthu timafunika kuugwira mtima
chifukwa masiku sachedwa kutha.
Masiku amathera kuchitseko.
-Masiku sachedwa kupita. Ukamakumana ndi mavuto ndi
bwino kudekha chifukwa masiku amavutowo akatha zinthu
zikhoza kukuyendera.
Masiku anadya atakumana.
-Ngakhale munthu atachita zoipa mwanseri, tsiku lina zimaza-
dziwika ndipo amachita manyazi.
Masiku ndi ambiri, ubweya wa nyama kuchepa.
-Tisamataye mtima nsanga, zabwino zili m’tsogolo.
Masiku sakoma onse.
-Nthawi zina timakumana ndi mavuto ndipo pena timakumana
ndi zabwino. Kukumbukira mfundo imeneyi kungatithandize
kuti tisamade nkhawa kwambiri zikativuta.
Maso a nyama ngofiira, sachedwa kutembenuka.
-Zinthu zimatha kusintha nthawi iliyonse, choncho tikakhala
pabwino tizikumbukira kuti zinthu zimatha kusintha nthawi ili-
yonse.
Maso a usiku anagona ndi wakhate.
-Pali zinthu zina zomwe sitingazidziwe, mwachitsanzo chifukwa
cha m’dima, munthu wina anagona ndi mzimayi wakhate. Osa-
masankha kuchita zinthu usanazimvetse bwinobwino.
Maso achule saopsa ovula nyanda.
-Tisamaope kuuza ena mavuto amene tikukumana nawo kuti
atithandize. Ngati tikudziwa zoonadi pankhani inayake si bwino
129