Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 129

Miyambi ya Patsokwe Mapundi amaphwanya mpini. -Olima mwamphamvu kwambiri amatha kuthyola mpini. Chimodzimodzi munthu wovuta kapena wandewu amakumana ndi mavuto chifukwa cha zochita zakezo. Masamba auma. -Mwambiwu umanenedwa pamene munthu wina waphwanya pangano. Masewera anabala mwana. -Nthawi zina zinthu zangati zongocheza zimatha kubweretsa mavuto aakulu. Ndiye ukaona kuti zayamba kusokonekera, ndi bwino kungochoka. Masewera sakhala paulimbo. -Osamachita chibwana ndi zinthu zomwe zikhoza kutiika m’mavuto. Masiku adalinda tsiku kufula. -Masiku akachuluka umakumana ndi mavuto ena. Umango- funika kulimbana nawo basi ndipo zimakuyendera. Masiku adameta Nkhanga mpala. -Nkhanga inayembekezera kwa nthawi yaitali kuti pangano loti ikametetse likwaniritsidwe. Ndi bwino kumasunga pangano lanthu. Masiku adatsutsa buthu. -Munthu akalakwa koma osafuna kuvomereza, nthawi imafika ndipo zimaululika. Masiku ali pakamchira kanyama. -Munthu usamataye mtima kuti zimene ukufuna zidzachitika kalekale chifukwa masiku sachedwa kutha. Masiku amaoletsa njovu. -Nthawi ikamapita, ngakhale zinthu zamphamvu komanso 128