Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 127

Miyambi ya Patsokwe ng’onayo chifukwa ikhoza kukuika m’kamwa. Si nzeru kuma- chitabe zinthu zomwe zingatiike m’mavito. Mano kunamiza. -Mawuwa amanena za munthu yemwe amakusekerera koma mumtima akukufunira zoipa. Mano saona umphawi. -Ngakhale munthu akhale wosauka, amafunikabe kudya. Zoti zithu zikuvuta kupeza, mano alibe nazo ntchito. Manong’onong’o amapha ubwenzi. -Miseche ikhoza kulekanitsa mabwenzi apamtima. Mantha ali n’kuseka, ukali uli ndi maliro. -Pamene munthu wachita mantha amathawa kuti adzipu- lumutse. Koma akalimba mtima kuthawira panja amakadyedwa ndi chilomo. Mantha anadyetsa n’nombwe. -Chifukwa cha kuopa zirombo anthu ena amaopa kukasaka nya- ma ndipo amangodyera zopanda pake ngati masamba a n’nombwe. Munthu ukamaopa kugwira ntchito yomwe ingakuthandize umphawi umakukwatira. Manunkhanunkha amapha mphuno. -Mawuwa amanenedwa pofuna kukhazika mtima anthu pansi, kuti asamangozunguzika ndi zilizonse. Manyazi adapha Lambe. -Lambe ndi mbewa yomwe sinkafuna kutuluka kunja chifukwa cha manyazi moti inafa ndi njala. Tisamachite manyazi kuchita zinthu zofunika. Manyazi anapha kamba. -Ukamasowa chinachake umafunika kulimba mtima. Kuchita mantha kapena manyazi kungachitise kuti tizingovutika ngati 126