Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 126

Miyambi ya Patsokwe m’malo mongotengeka ndi zimene otsatsa malondawo akunena. Malunje sadya Sakhwi. -Tisaope tikafuna chinthu chifukwa cha kuwopsedwa ndi maon- ekedwe a chinthucho. Si bwino kuopa kunena vuto lathu kuti anthu atithandize. Mamveramvera amapasula banja. -Osamangotengeka ndi zonena za anthu. Mamveramvera anachotsa zolo paukwati. -Kumangomvera zonena za anthu kukhoza kutitayitsa mwayi. Komanso potumiza anthu kuti akatiyimire, tizitumiza okhulupi- rika kuti nkhani isasokonekere. Manda a mkonzi sakhala akuya. -Nthawi zina ngakhale munthu ukhale wabwino chotani pamudzi anthu sayamika. Munthu wina wokumba manda anka- thandiza anthu pakachitika maliro. Koma atamwalira anthu anangokumba moti athane nazo ndipo anangolekera m’maondo. Manda sakana maliro. -Manda alibe tsankho, amalandira olemera ndi osauka omwe. Mankhwala a utsi n’kuthawa. -Munthu ukafuna kupewa zinazake kapena ngati zinazake sizikukusangalatsa ndi bwino kungochokapo. Mankhwala amalimba ndi chizimba. -Mawuwa amatanthauza kuti mlandu umazengedwa bwino pa- kakhala mboni kapena umboni wooneka bwino. Mano a Ng’ona umawaona bwino uli m’kamwa mwa Ng’onayo. -Ndi mano ochepa omwe amaonekera pakamwa pa ng’ona. Kungakhale kupanda nzeru kusuzumira kuti uone mano onse a 125