Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 125

Miyambi ya Patsokwe zawo n’kusokonekera. Makondamakonda, Buluzi anakonda khonde. -Zokonda zimasiyanasiyana, choncho mnzathu akamakonda zi- nazake, tisamuseke chifukwa zokonda zathunso zikhoza kukha- la zoseketsa kwa anthu ena. Makutu achitirana nsanje. -Sizingatheke kumamvetsera munthu ndi khutu limodzi, linalo n’kumamvetsera wina. Umafunika kumvetsera m’modzi kaye. Kuchita zinthu ziwiri sikuthandiza. Makutu sakhuta ndi kumva, maso sakhuta n’kuona. -Sitingakwanitse kupeze zonse zimene timaona kapena kumva. Ndi bwino kumakhala okhutira. Malawalawa anapha milomo. -Tiyenera kuchenjera ndi zinthu zomwe timakonda chifukwa pamapeto pake chikhoza kutiika m’mavuto. Maliro m’mbale. -Mawuwa amatanthauza ndiwo za nyama. Maliro n’kulirana. -Zovuta zikachitika kapena mavuto akabwera timayenera kuthandizana. Malonda ali m’maso. -Munthu umafunika uyambe kaye waona malonda usanagule. Malonda amakoma ndi kugulana. -Zinthu zimayenda bwino anthu akamathandizana. Malonda amakoma ndi n’kuikira (banyira). -Wamalonda akamapereka banyira, anthu ogula amamukonda. Malonda ndi m’maso, pakamwa pamangotenderera. -Munthu ukamafuna kugula kanthu umafunika uchionetsetse 124