Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 124

Miyambi ya Patsokwe Makale sapangana adalira m’thumba. -Pamakhala chinthu choululitsa zobisika kapena zachinsinsi. Makale sapangana. -Mawuwa amanenedwa pamene anthu awiri apita kumlandu asanapangane kapena kugwirizana chokanena. Makani sawombola munthu. -Kumva zako zokha kukhoza kuika munthu pamoto. Munthu amayenera kumamva malangizo a ena. Mwayi umakupeza uli pabwino kale. Makasu akalira ndiye kuti alipo awiri. -Tiyenera kumathandizana ngati tikufuna kuti tichite zakupsa. Mako ndi mako angachepe mwendo. -Osamanyoza makolo ngakhale atakhala kuti ndi osaoneka bwino. Chikondi cha pachibale sichitha. Mako ndi mako usawaone kuchepa mwendo. -Osamanyoza makolo ngakhale atakhala kuti ndi osaoneka bwino. Chikondi cha pachibale sichitha. Tizipereka ulemu kwa makolo ngakhale ali onyozeka. Makolo amasamalira ana mano awo akamamera, ana amasa- malira makolo mano awo akayamba kuguluka. -Ndi bwino kumasamalira makolo chifukwa nawonso anavutika kutisamalira tili ana. Makolo amasamalira ana, mano a anawo akamamera; pomwe ana amasamalira makolo awo, mano a makolowo akayamba kuguluka. -Ana ali ndi udindo wosamalira makolo awo akamakalamba. Makolo atsoka amati, “ndinadya chiyani ine kuti ndibereke chitsilu ngati chimenechi?” -Pali ana ena omwe ngakhale tiwalele bwino, amatha kuyamba 123