Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 123

Miyambi ya Patsokwe Madzi saiwala khwawa. -N’kovuta munthu kuleka chizolowezi chake. Si bwino kuiwala makolo kapena zinthu zina zofunika. Madzi saiwala mkolokolo. -Si bwino kuiwala makolo kapena zinthu zina zofunika. Anga- tanthauzenso kuti zimakhala zovuta kuiwala zimene unazolow- era. Mafukufuku sayenda, imayenda ndi nyama. -Ngati wafunsira mkazi amayembekezera kuti uzimuyendera kuti adziwe kuti umamukondadi. Munthu akabwereka ngongo- le umamupitira kwawo chifukwa kawirikwawiri sangabwere kudzakupatsa ndalama yako. Mafuta amagwera pa anzake. -Ulemerero umabwera pamene pali ulemerero kale. Mwayi umakupeza uli pabwino kale. Magulugulu a mvula anathawitsa mkamwini kumudzi mvula isanagwe. -Si bwino kumataya mtima msanga tikakumana ndi mavuto kapena tikamva zinazake zokhumudwitsa. Tisamapupulume kuchita zinthu tisanamvetse bwino nkhani. Magwiragwira amapha manja. -Kugwiragwira kumabweretsa mavuto. Maimvaimva adathawitsa zolo paukwati. -Mamveramvera amabweretsa zowawa. Ndi bwino kuchita zin- thu zimene ukuona kuti zikuthandiza m’malo momvera anthu ena. Maimvaimva amapha makutu. -Si bwino kumangokhulupirira zonena za ena tisanafufuze bwinobwino. 122