Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 122

Miyambi ya Patsokwe Madzi akataika sawoleka. -Zinthu zikataika kapena zikasokonekera, zimakhala kuti zasokonekera basi. Madzi akatayika sawoleka. -Pali zinthu zina zomwe zikachitika, sizingathekenso kuzibwe- zeretsa. Madzi amachuluka ndi a m’njira. -Zinthu zazikulu zimayamba pang’onopang’ono, monga mtsinje umadzadza ndi madzi a m’ngalande. Madzi amakoma akakhala m’chinkho, koma akakhala mumtsinje amapha. -Pali zinthu zina zoopsa zikakhala malo ena kapena zikakhala zambiri. Madzi apamwala amatunga ndi amene walawira. -Ukafuna kuchita chinachake umafunika kuchita zinthu mofu- lumira. Ulesi umamanitsa zambiri. Madzi apamwala watunga walawira. -Ukafuna kuchita chinachake umafunika kuchita zinthu mofu- lumira. Ulesi umamanitsa zambiri. Madzi n’kulubza, mchenga upita pansi. -Mawu onenedwa ndi anthu awiri odziwana kuti amuchenjerere munthu wina. Madzi ndi moyo. -Madzi ndi ofunika kwambiri pa moyo wa munthu. Madzi odikha ndi amene amalowa pansi. -Munthu waphee ndi amene amakhala ndi maganizo akuya kapena oopsa. Madzi oyera umasambira kumutu, akuda kumapazi. -Alendo mumawapatsa zabwino, zinazo zimakhala zanu. 121