Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 121

Miyambi ya Patsokwe M’thunzi umodzi suthera nkhani. -Ndi bwino kukhala odekha m’malo mopupuluma kuti zinthu zina zithe mwachangu. M’tsuko sulowa m’chiko, koma chikho ndicho chimalowa mumtsuko. -Munthu waudindo ndi amene amapatsidwa ulemu, koma iyeyo sachita zimenezo kwa ena omwe ndi otsika. M’yang’ana dzuwa adasochera. -Ngati tikukayika kapena sitikudziwa zoyenera kuchita ndi bwino kufunsa kuti tichite zinthu moyenera. Mabatani akunsana amakumanga ndi anzako. -Timafunika kuthandizidwa ndi anthu ena. Mabingu a mvula anathawitsa mkamwini kumudzi mvula isanagwe. -Osamapupuluma kusiya kuchita zinthu chifukwa cha zinthu zomwe sitikutsimikizira ngati zingachitikedi. Machokero a pabwalo. -Munthu akatsanzika kuti akubwera kukatenga chinachake ndiyeno osabweranso, anzake amanena kuti, “anangonama kuti akukatenga chinthu, anali machokero a pabwalo.” Madoli (matodwe) adafera mchenga woyera. -Zinthu zina zimangokongola m’maonekedwe zili zosathandiza kwenikweni. Madoli anafera mchenga woyera. -Pali zinthu zina zomwe zimaoneka zabwino zomwe pambuyo pake zikhoza kutiika m’mavuto. Madzi adzadza, mlamba usangalale. -Munthu ukapeza zinthu zabwino umafunika kusangalala. 120