Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 120

Miyambi ya Patsokwe M’mera m’poyamba. -Ndi bwino kumachita zinthu moyambirira. Ngati ukufuna kuti ana ako akule bwino, ndi bwino kuyamba kuwalangiza kuyambira ali aang’ono. Kuti tidzakolole zambiri, timafunika kudzala moyambirira. Kuchita zinthu moyambirira n’kofunika kwambiri. M’mimba ndi m’chipala. -Ngakhale ana obereka mayi m’modzi amatha kukhala osiyana m’maonekedwe, makhalidwe komanso zochita zawo. Pa chipala ndi pamene amasulira zinthu zosiyanasiyana monga makasu, mipeni, zikwakwa ndi zina. M’mphechepeche mwa njovu sapitamo kawiri. -Ngati munthu wapulumuka pa vuto mwamwayi, si bwino kubwereza kuchitanso zomwezo. M’mwemo anakhazikitsa tsindwi pakhudu (pambali). -Munthu waulesi amawononga zinthu ngakhale zake zomwe. M’nyumba mukasowa ufa, sataya mkute. -Tisamawononge zinthu zathu ngakhale titakhala pabwino, chifukwa tikhoza kudzazifuna mawa. M’nyumba yamwini saotcheramo mbewa. -Si bwino kumachita chilichonse chomwe timachita kwathu tikapita kuchilendo chifukwa mwina eni akewo sasangalala nazo. M’thengo saikizamo bowa. -Munthu ukakhala ndi chinthu ndi bwino kuchisamala chifukwa ukapusa anzako akhoza kukutolera. M’thumba lamwini sapisamo dzanja. -Osamayamba zinthu podalira ndalama za m’thumba la munthu wina. 119