Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 116

Miyambi ya Patsokwe Ladza dzinja, ana anole mano. -Mavuto akakupanikiza kumakumbukira kuti amatha ndipo chi- sangalalo chimabwera. Lakoma thendo, nyama ilowa m’mano. -Nyama ndi yokoma kwambiri koma kuipa kwake imalowa m’mano. Munthu akakhala ndi moyo wosalira zambiri savutika. Lambulire, nawe ndidzakulambulira. -Zinthu zimayenda mukamathandizana. Laponda diwa lamphawi. -Nthawi zina munthu amapeza mwayi womwe sama- yembekezera. Lekani! manong’onong’o adadzutsa njovu. -Zinthu zazing’ono zimatha kuyambitsa zazikulu. Mwachitsanzo, phokoso laling’ono lingachititse kuti njovu idzu- ke n’kupha anthu. Lende n’kukankhana. -Mnzako akukuchitira zabwino nawenso ndi bwino kumuchitira zabwino. Katungwe n’kukankhana. -Zimakhala bwino kumathandizana. Lero lomwe lidadetsa Nthengu. -Nthawi zina ndi bwino kudikira pochita zinthu chifukwa tikachita mofulumira nthawi zina zinthuzo sizichitika bwino. Kuchita zinthu modekha kumathandiza kuti zinthu zisasokon- ekere. Mwachitsanzo, nthengu inkafuna kuti aimalize kuipenta tsiku lomwelo. Chifukwa chosafuna kubweranso mawa, anai- paka penti wakuda. Lero muchira ndi madzi okha. -Mkuluwikowu umatanthauza kuti pakhomo palibe chakudya. 115