Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 115
Miyambi ya Patsokwe
Kwanu sikutalika.
-Kwanu kungatalike bwanji, umachita zotheka kuti ukafikeko.
Kwapsa kwamera, koma kwatsala thengo.
-Zinthu zikachitika sizitheratu, mwachitsanzo mlandu ukhoza
kutha koma anthu n’kumasungiranabe chakukhosi.
Kwatsala tchire moto umapita komweko.
-Chaona mnzako lero mawa chidzaona iwe.
Kweza Mbawala m’mwamba.
-Osamadziika dala m’mavuto pokhala dala pamalo oipa kapena
kuchita zosayenera.
114