Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 113

Miyambi ya Patsokwe kulemekeza amene amatisamala ndi chinthu chofunika kwambi- ri. Kuzingwa kwa Kalulu kukapsa. -Anthu ambiri amakhala osangalala ngakhale ndi zochepa zom- we ali nazo. Koma zimene amadalira monga makolo akamwali- ra, amakhala m’mavuto aakulu, osowa nawo pothawira. Kwa amake a mwana ndiko kuli madyera. -Mwana kapena munthu aliyense amasangalala kwa amayi ake chifukwa mayi sanganyoze mwana wake. Kwa ena n’chitsiru, amake ati mwana. -Makolo amakondabe ana awo ngakhale atakhala ndi mavuto ena. Kwa eni kudyetsa nthanga dzungu ukulifuna. -Munthu ukakhala kwa eni umakhala wopanda ufulu wochika kapena kuyankhula chilichonse chimene ukufuna. Tiyenera ku- khala odzichepetsa tikakhala kwa eni. Kwa eni kuika moyo, kuipira kudwala. -Ukakhala kwa eni umapulumuka zoipa zochokera kwa abale, koma ukadwala umakumbukira kwanu. Kwa eni kulibe “mkuwe,” ukakuwa wadzikuwira nkhondo. -Munthu ukakhala kwa eni sumalamulira, ukachita zimenezi amatha kukuthamangitsa. Kwa eni kulibe mkuwo, mutu wa nkhuku n’chiwalo. -Ukakhala kwa eni umachita zomwe kwanu sukanachita monga kudya mutu wa nkhuku pomwe kwanu umadya ziwalo zofewa. Kwa eni kusunsitsa msuzi ndiwo ukuzifuna. -Munthu ukakhala kwa eni umalephera kuchita zomwe ukadachita uli kwanu. 112