Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 110

Miyambi ya Patsokwe Kutsutsa ngomwa n’kuivulira. -Potsutsa munthu umafunika kukhala ndi umboni weniweni. Kutukwana samangira mtanda. -Munthu uyenera kumachita manyazi ukapanga chinthu cholakwika. Kuuma kwa mutu kumachititsa kuti pakamwa patsegule m’mimba. -Anthu opanda nzeru ndi amene amalongolola kwambiri. Kuutsa mapiri pachigwa. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wachititsa kuti anthu ayambane, kaya ndi apachibale kapena ena adera. Kuvala khoza ndi kuwolowa dzanja. -Khoza ndi chibangiri. Kuti munthu avale chibangiri amafunika kufewetsa dzanja lake. Kuti munthu azikondedwa kapena ku- patsidwa zinthu amafunika kukhala wopatsa. Komanso munthu wopatsa sachita kudikira kuti ena amupemphe kuti awathan- dize. Kuwerengera madzi a mphutsi. -Mayi wina amawiritsa madzi kuti aphere mphutsi, koma mlen- do ankaganiza kuti ndi madzi a nsima. Mawuwa amatanthauza kuwerengera zinthu zosakhala zenizeni. Kuwerengera mbewa ndi michira yomwe. -Kuwerengera ndi zinthu zoti palibe zomwe. Kuweta Galu ndi kum’ponyera chakudya. -Mwambiwu umatanthauza kuti kuti munthu akhale ndi ana kapena anthu ena, amafunika kuwadyetsa komanso kuwasama- lira. Kuwongola mtengo mpoyamba. -Kuti munthu akhale ndi makhalidwe abwino ayenera 109