Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 109
Miyambi ya Patsokwe
Kuti ndidye ndiponda muno, otsala ngam’kamwa.
-Mwambiwu m’Chichewa chamakono umanena za munthu
amene akunena kuti, “Kuti ndipeze chakudya ndiponda muno,
sindikusamala zomwe anthu atanene chifukwa angokhala
am’kamwa.” Tisaleke kuchita zinthu zofunikira poopa
manong’onon’go. Anthu sadzaleka kunong’ona akaona wina
akuchita zinazake.
Kutola fulu ndi kulawira.
-Ngati munthu ukufuna kugwira ntchito bwino ndi bwino ku-
lawira.
Kutola khobwe n’kum’mawa.
-Munthu akafuna kuchita chinthu amafunika kuchichita mwan-
sanga.
Kutola khobwe ndi m’mawa.
-Tisamazengereze tikafuna kuchita kanthu. Tisamachedwe
pochita zinthu ngati omwe akukolola khobwe, akachedwa khob-
we yense amathera pansi n’kuthetheka. Tikafuna kugwira ntchi-
to ndi bwino kulawira kapena kuchita moyambirira n’kufunika.
Kutola nkhwangwa ndi mpini womwe.
-Mawuwa amanenedwa pamene munthu wachita mwayi
waukulu kwambiri umene samayembekezera.
Kutola si kuba.
-Kutola kanthu si kuba, koma ukatenga pakhomo pa munthu
osapempha.
Kutsutsa Galu n’kukumba.
-Ngati munthu akukana kuti sanalakwe pamafunika kukhala
mboni yoti imutsutse. Si bwino kutsimikizira chinthu usadapeze
umboni wokwanira.
108