Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 108

Miyambi ya Patsokwe Kutapa nzeru m’thumba la Likongwe. -Mawuwa amanena za munthu amene amayamba kaye wafunsa ena asanachite zinthu. Kuchita zimenezi kumathandiza munthu kuchita zinthu mwanzeru. Kutaya udzu womwetamweta. -Mawuwa amatanthauza kutaya mwayi wopezapeza. Kutchena ndi kupirira. -Kuti atsikana kapena azimayi atchene, kaya ndi m’mutu, ama- funika kupirira ululu. Mwachitsanzo, ena amapsa ndi livuloni koma samasiya. Kutemetsa nkhwangwa pamwala. -Kutaya mwayi pogwiritsa ntchito chinthu mosayenera. Mawu- wa angatanthauzenso kukanitsitsa. Kutengera zinthu pamgong’o. -Kutenga zinthu udyo kapena kumva zinthu molakwika. Si bwino kumazezeduka kapena kumajijirika kwambiri. Kuthamanga sikufika. -Kuchita zinthu mofulumira kwambiri kumabweretsa mavuto kapena kuwonongetsa zinthu. Kuthawa mtswatswa wako womwe. -Kunamizira kukana chinthu chomwe wachita ndiwe wemwe. Kuthawa ndewu si mantha, koma kusamala mano. -Kupewa zinthu zobweretsa mavuto ndi nzeru kusiyana ndi kuzichita n’kupeza mavuto. Kuthyola ndiwo n’kuwerama. -Munthu akafuna kupeza zinthu amafunika kugwira ntchito molimbika. 107