Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 107

Miyambi ya Patsokwe Kusamala mano si kutsuka mkamwa kokha, komanso kupewa zigogodo. -Ndi bwino kumapewa ndewu chifukwa zimabweretsa mavuto. Kuseri kulinji? -Ngakhale mafumu amanyozedwa kumbali. Munthu sungadzi- we zomwe ena amanena kuseri. Kuseri kumvenji? -Munthu ukakhala pawekha zambiri zimakupita. Kuseri kutukwanitsa a Chiwere. -Ngakhale mafumu amanyozedwa kumbali. Munthu sungadzi- we zomwe ena amanena kuseri. Kuseri kwecheche, adagwidwa msanasana. -Pakhalekhale choipa chilichonse chimene chimachitidwa mseri, chimadzaonekera poyera. Kusiya fumbi. -Limeneli ndi bodza lonenedwa ndi munthu nthawi yamavuto. Nthawi zinanso angatanthauze kupulumuka pamlandu chifu- kwa chodziwa kuyankhula mochenjera. Angatanthauzenso kuthawa ndi liwiro lalikulu. Kusiya n’kute n’kulinga utatolatola masana. -Mwambiwu umatanthauza kuti munthu amene amapeza zo- chepa, sakhala ndi zambiri zosunga. Kusochera ndiko kuphera kulupsa. -Akamati munthu wataika ndiye kuti wachita zinthu zomwe sumafuna kuchita kapena walephera kuchita zomwe amafuna. Kuswa mtedza chokhala n’kwabwino. -Kuti ntchito igwirike bwino pamafunika kuifatsira. 106