Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 106

Miyambi ya Patsokwe tinaganiza zoti tikaimangirire pamtengo uwo. Taonani msipu wake ukungoti biriwiribiriwiri, kukongola. Zoona mbuziyi ife ndi njala msipu uli m’khonde?” Mwini mbuziyo atamva zimene- zi anawakhulupiriradi. Koma mbuziyo inkadziwa kuti anthuwo akunama. Ndiye chifukwa choti sitha kuyankhula, akubawo anapulumukira m’kamwa mwa mbuzi. Kuputa ndewu n’kuimirira. -Munthu amene akufuna kumenyana ndi mnzake amati aka- yamba mnzake amaimirira kuti amenyane naye. Ukamayamba kuchita chinthu umafunika kukhala ndi zonse zokwanira kuti izimalizitse. Ukamawaputa mavuto umafunika kulimba nazo. Kuputa Vumbwe n’kulinga uli ndi Nkhuku. -Kuti anthu azikonda kubwera pakhomo umafunika ku- mawadyetsa bwino. Ukamaputa chinthu umafunika kumakhala ndi podalira. Kusadziwa n’kufa komwe. -Munthu ukakhala mbuli palibe chingakuyendere. Kusafunsa kudadyetsa njuchi. -Kufunsa kumathandiza kuti tisakumane ndi mavuto. Kusafunsa kudamwetsa posamba. -Kufunsa kumathandiza kuti tisakumane ndi mavuto. Kusafunsa kudaphikitsa tsabola. -Kufunsa kumathandiza kuti tisakumane ndi mavuto. Kusafunsa kudapsetsa Tambala. -Kufunsa kumathandiza kuti tisakumane ndi mavuto. Kusalowa m’nyumba salumbira. -Munthu sunganyanyale kuti sudzachitanso chinthu chomwe chili chofunika kwambiri pamoyo wako, monga kulowa m’nyumba mwako. 105