Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 105

Miyambi ya Patsokwe Kupha Njoka n’kumutu. -Kupha njoka kumafuna kuimenya mutu. Kuthetsa nkhani n’kulinga utadziwa chimene chayambitsa. Kuphera Nkhumba pamsikiti. -Kuchitira ena zinthu zosayenera komanso zolakwika malinga ndi chikhalidwe kapena mwambo wawo. Kuphunzira kumakathera kumanda. -Pa moyo wa munthu pamakhala zambiri zoti uphunzire ndipo umaphunzirabe mpaka kudzamwalira. Ena amati kumwalirako ndi phunzironso palokha. Nanga umakhala kuti unamwalirapo ngati? Umaphunzirira pomwepo kumwalira. Kuphunzira sikutha. - Pa moyo wa munthu pamakhala zambiri zoti uphunzire ndipo umaphunzirabe mpaka kudzamwalira. Ena amati kumwalirako ndi phunzironso palokha. Nanga umakhala kuti unamwalirapo ngati? Umaphunzirira pomwepo kumwalira. Kungoti kumatha ukakhala kuti wamwalira. Kupsa n’kupsa thuza. -Kawirikawiri zolakwa zazing’ono tikaziikira mang’ombe zimaoneka zazikulu. Kupulumukira m’kamwa mwa mbuzi. -Kupulumuka pa mlandu chifukwa chonena bodza. Nkhani yake imati, tsiku lina anyamata awiri anapeza mbuzi itaman- gidwa pamtengo wina ndipo anaganiza zoti aibe. Atangoyamba kumasula chingwe cha mbuziyo, mwini wake anabwera ndipo anawafunsa kuti, “N’chifukwa chiyani mukumasula mbuzi yanga?” Anthuwo anayamba kuchita mantha. Koma m’modzi anati, “Tinaona kuti pano palibe msipu wabwino, ndiye 104