Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 104

Miyambi ya Patsokwe Kupatsa n’kuyikiza. -Ukamathandiza anzako, nthawi ina nawonso amadzakuthandi- za. Kupempha si kuba. -Kuuza munthu kuti akuthandize si kulakwa. Kupenya kumwamba n’kukhala ndi Nkhuku. -Munthu ukakhala ndi chinthu umayesetsa kuchiteteza monga munthu akakhala ndi Nkhuku amayesetsa kuziteteza kwa Mphamba. Kupenya pawiripawiri kudathyola khosi. -Ndi bwino kusankha kuchita chinthu chimodzi m’malo mochita zambirimbiri nthawi imodzi. Kupepera kulibe mankhwala. -N’zovuta kusintha kapena kuthandiza munthu wopepera. Kupha Galu wachiwewe n’kulelemeza mpini. -Pofuna kugwira munthu wochenjera kwambiri pamafunika ku- mufatsira komanso kumutenga bwino. Kupha mbalame ziwiri ndi mwala umodzi. -Kupeza mwayi waukulu kwambiri mosayembekezereka. Kupha Mkango ndi kuweteka. -Pofuna kuchita zinthu pamafunika kufatsa ndi kupeza nzeru yeniyeni. Kupha n’kupha umakumbuka poguza. -Tisanayambe kuchita chinthu tiziyamba tadzifunsa kuti, ‘Kodi zimenezi zitha bwanji?’ Kupha Njoka n’kudula mutu. -Kupha njoka kumafuna kuimenya mutu. Kuthetsa nkhani n’kulinga utadziwa chimene chayambitsa. Kuti uthane ndi vuto umafunika kuthana ndi chimene chikuyambitsa vutolo. 103