Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 103
Miyambi ya Patsokwe
Kuonda saombezera.
-Ngati takumana ndi mavuto, tisamathamangire kuloza ena
zala.
Kuonera patali, nyani anadzipha yekha.
-Si bwino kumangotengera zinthu zomwe sukuzidziwa bwinob-
wino kapena chifukwa c choona kuti ena zikuwayendera.
Kuonerana m’kodi.
-Mawuwa amatanthauza kunyozana, kudererana kapena ku-
chitirana mwano.
Kuonerana m’madzi.
-Mawuwa amatanthauza kunyozana, kudererana kapena ku-
chitirana mwano.
Kuopa n’kukhala pambuyo ngati mchira.
-Munthu amene akufuna kuchita bwino ayenera kuona mmene
ena akuchitira.
Kupata kumasiyana.
-Anthu amapeza zinthu mosiyana, ena amapeza zambiri kuposa
anzawo.
Kupata n’kosiyana.
-Anthu amapeza zinthu mosiyana, ena amapeza zambiri kuposa
anzawo.
Kupatsa n’kudzala, kunama n’kukazinga.
-Ukathandiza mnzako umakhala ngati wadzala, mawa
adzakuthandiza iweyo.
Kupatsa n’kuika, kunama n’kukazinga.
-Ukathandiza mnzako umakhala ngati wadzala, mawa
adzakuthandiza iweyo.
102