Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 102

Miyambi ya Patsokwe anthu. Kunkira nsale n’kumodzi. -Nsale ukamakula umakulira kofanana. Nafenso tizichita zinthu mogwirizana komanso mofanana kwambiri ngati amodzi. Kuno n’kunja kudayanja lichero. -Ukalemera usamanyoze anzako, zamawa sizidziwika. Kunong’oneza bondo. -Mawuwa amatanthauza kudandaula utakumana ndi mavuto chifukwa cha kusamva kapena kunyalanyaza machenjezo. Kunyaza Katumbu n’kuvuula mono. -Katumbu amakonda kuba msomba m’mono. Kuthana naye n’kungovuula monowo. Chimodzimodzinso ndi ena omwe amachita zinthu zosokoneza monga kuba, kuti uthane nawo umafunika kumatseka chitseko chako ndi loko. Kuolokera pakangaude. -Kukhala ndi mwayi wopulumuka m’mavuto mosadziwika bwino. Kuombera mapira pamutu. -Kuchenjerera mnzako pomubisira zoyenera kuchita kapena kusamuuza zoona zenizeni. Kuona chidameta Nkhanga mpala. -Kukumana ndi mavuto kapena kukhaula. Kuona Fisi si kubadwa kale. -Mawuwa amatanthauza kuti ngakhale mwana akhoza kudziwa zambiri kuposa munthu wamkulu. Kuona maso a nkhono n’kudekha. -Kudekha komanso kuugwira mtima kumathandiza kuti upeze zabwino. Munthu wofatsa amadziwa komanso kuona zambiri kuposa munthu wopupuluma. 101