Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 100

Miyambi ya Patsokwe mnzeru kuti ena akadzamwalira zinthu zisadzaime. Mwambiwu unachokera pa mawu omwe anthu ena ankanena akamafuna kuti wina awafunire mankhwala. Ankangoti, “Mukatikumbire mankhwala.” Anapitiriza kupemphabe mpaka munthuyo anamwalira. Akanakhala anzeru akanafunsa munthuyo kuti awauze mitengo yake kuti azikakumba okha. Kumbuyo kulibe maso. -Zimene zinachitika kale sitingazisinthe. Tiyenera kumaganizira zam’tsogolo zomwe tingazisinthe. Kumene kutalire n’kunsonga. -Mawuwa amatanthauza kuti amene atagonje ndi wamng’ono. Anthu akamamenyana, amene amayamba kulira ndi ana ndiye anawo akuyerekezedwa ndi kunsonga. Mawuwa amanenedwa pamasewera poderera ena kuti ndi ana. Kumeneku n’kukonza chitseko chimera chitatha. -Mawuwa amanenedwa poseka munthu wozengereza. Ena amazengereza kupalira m’munda. Mbewu zawo zikayamba kuwonongeka mpamene amayamba kupalira. Ena angamaone kuti chimera chawo chikubeda, koma n’kumangonyalanyaza. Akamaganiza zoti akonze chitseko chawo, amapeza kuti chime- ra chija chatha. Kumira pachipande. -Mawu okokomeza omwe amatanthauza kuti munthuyo akuna- ma mopanda manyazi. Kumva mawu a akulu n’kuchezera. -Mawuwa amatanthauza kuti, kuti munthu amve zimene aku- luakulu akukambirana amafunika kukhala maso osagona. Ame- ne akufuna zinthu zimuyendere ayenera kumvera zimene aku- luakulu akumuuza chifukwa aona zambiri pamoyo wawo. 99