Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 99

Matigari Ndinatero. Koma iye anandiyankha kuti: ‘Ayi, sindikunena zim- enezo. Ndikunena za anthu omenyera ufulu wawo omwe anathawira kunkhalango. Abweransotu. Anthu olimba mitima aja abweranso ndithu.’ ‘Mwandimanga m’masambatu pame- nepo. Chachitika n’chiyani?’ Ndinamufunsa choncho. ‘Kodi un- gakhulupirire? Ndi munthu wamfupi kwambiri. Ndati chiyani? Ndi wamfupi. Ndi wamfupi ngati chitsa ndipo anavala chisoti chozika nthenga komanso ananyamula chijasi chachikopa cha kambuku paphewa pake. Koma kenako anangosintha n’ku- sanduka chiphona. Ndikutitu chiphona! Anaima ngati Goliyati n’kuuza wapolisi yemwe anali ndi galu kuti: ‘Ndine Matigari ma Njiruungi, ndipo ndikukuchenjeza, musiye mtsikanayo msanga!’ Kodi ndingafotokoze bwanji? Mawu ake anali ngati chiphaliwali. Galu amafuna kuluma mtsikanayo anachita man- tha n’kupsatira mchira wake. Kodi unayamba wamvako zangati zimenezi?’ Pamene amandiuza zimenezi ndinangoona moto ukuphulika kufakitale ndipo ndinadziwa kuti kwaipa. Ogwira ntchito amawotcha ziboliboli za a Boy ndi a Williams zomwe zi- nali panja pafakitaleyo. Ogwira ntchitowo anasangalala kwam- biri kuona zibolibolizo zikunyeka ndi moto. Kenako ndinamva mawu a Ngaruro wa Kiriro omwe anatengedwa ndi mphepo pomwe amayankhula pa chinkuzamawu. Mundimvetsetsetu pano, ndangogwira mawu ake omaliza. Anati: “Atsamunda amenewa komanso antchito awo ayenera kulongedza katundu wawo azipita kwawo. Anthu okonda dziko lawo, a Matigari ma Njiruungi, abweranso ndipo ogwira ntchito ayenera kugwiri- zana ndi Matigari. Wodzala ayenera kukolola mbewu zake! Ife takana kukhala ngati mapoto omwe amaphika koma osadya na- wo!” 98