Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 97

Matigari “Anzanganu munandifunsa funso, koma sindinaliyankhe. Mwachidule ndinene kuti: Ndapezeka kuno chifukwa malinga ndi zimene akunena, akuti ndilibe chikalata chosonyeza kuti nyumbayo ndi yanga. Koma tandiuzeni, kodi munthu angafu- nenso chikalata chamtundu wanji kuposa thukuta komanso magazi omwe ndinakhetsa kungochokera pamene tinayamba kuyedzeka maziko a nyumbayo mpaka khoma kumakwera? Ko- di tilowere kuti ife anthu omenyera ufulu wa dziko lathu, ife a Matigari ma Njiruungi?” “Matigari ma Njiruungi?” anthu awiri omwe anali asa- nayankhule aja anakuwa nthawi imodzi. “Kodi ndinu amene chakumasanaku munalanditsa mtsikana kuchokera m’kamwa mwa galu wolusa uja?” Anthu ena onse aja anadabwa kwambiri atamva zimene an- thuwa ananena. “Kodi ndinu munthu amene Ngaruro wa Kiriro amanena kufakitale kuja apolisi asanabwere n’kuyamba kuthyola dzipala- pasiro za ogwira ntchito?” m’modzi mwa anthu anayankhulira limodzi uja anafunsa. “Apolisi asanabwere n’kuyamba kuthyola dzipalapasiro za ogwira ntchito? Liti? Lero?” ena omwe anali museloyo anafunsa akuyang’ana munthu yemwe ananena zimenezi uja. “Kodi simunamve mmene apolisi atibulira anthu kufakitale lero?” “Nanunso tatiuzani chimene chachitika kuti mupezeke kuno.” “Onse anakhala tsonga n’kuimika makutu akuyang’ana munthu ankayankhula uja pamene ankayamba kufutukula nkhani yake.” 96