Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 96

Matigari “Kenako ndinatopa nazo moti ndinayamba kulimbana ndi Mtsamundayu chifukwa cha zimenezi.” “Ndinalumbira kuti ndidzamenyera nkhondo ufulu wanga komanso wadziko langa mpaka nditamupirikitsa. Tsiku lina ndinapita kwa Mtsamunda Williams n’kumuuza kuti alongodze katundu wake n’kutuluka m’nyumba yanga ndipo ndinamu- lozera nsana wanjira yakwawo. Ndinamuuza kuti, ‘Pita ukamange yako nyumba. Nawenso manja uli nawo ako.’ Koma anagwira chiputu. Sankafuna kutuluka. Kenako anathamangira kumene kunali lamya ndipo ine ndinathamangira kumene kunali mfuti. Koma kodi mukumudziwa amene anandulumphi- ra akukuwa kuchenjeza Mtsamunda Williams? Analitu John Boy! Nditalimbana naye, ndinamupulumuka m’manja n’kutha- wa kudzera pazenera kupita kumapiri. Mtsamunda Williams ndi John Boy anayamba kundisakasaka. Tinalimbana kwa zaka zambiri ndipo tinkangokhalira kusakanasakana paliponse. Ndi- nayamba ndi kuzimitsa John Boy. Ndipo dzulodzuloli ndathana ndi Mtsamunda Williams. Ndinamuonetsa zoopsa moti kenako ndinamuponda pachifuwa nditakweza zida m’mwamba kutsimikizira kuti ndamulumitsa mano. Popeza ndinali ndita- pambana nkhondo, ndinaganiza zobwerera kwathu kuti ndi- katenge nyumba yanga.” “Abale anga! Simungakhulupirire malodza amene ndinaona nditafika kunyumba yanga ija! Mukuganiza kuti ndi ndani ame- ne ndinamupeza ataima pageti la nyumba yanga? Mwana wa John Boy komanso wa Mtsamunda Williams! Pamenepo mpamene ndinazindikira kuti mwana wa Boy ndi amene anatenga makiyi a nyumba yanga. Kenako anakoka chingwe kupolisi moti posakhalitsa apolisiwo anatulukira n’kundigwira. Kodi chilungamo chili kuti m’dziko lino makosana?” 95