Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 94

Matigari akuwerenga Baibulo pagome. "Ndiyeno nthawi ya chakudya chamadzulo itafika, anakhala pagome limodzi ndi ophunzira ake. Iye anawauza kuti: Ndi- nalakalaka ndithu kudya chakudya chimenechi pamodzi ndi inu, pakuti ndinena ndi inu, sitidzadyanso limodzi chonchi ku- fikira Ufumu ukadzabwera. Ndipo mmene adatenga mkate, na- yamika, anaunyema, anawapatsa n’kuwauza kuti: Ili ndi thupi langa lopatsidwa chifukwa cha inu; chitani ichi chikumbukiro changa kufikira ndidzabwerenso kachiwiri. Kenako anatenga chikho, ndipo pamene anayamika, anati, chikho ichi ndi pan- gano latsopano la pakati pathu chifukwa cha magazi athu. Muzi- chitirana zimenezi kufikira ufumu udzabwere, mogwirizana ndi chifuniro chanu.” Wamowa uja anasiya kuyankhula. Kenako anatembenukira kwa Matigari: “Tatiuzeni zoona. Kodi inuyo ndi ndani? Chifukwatu sindi- naonepo munthu atalowa m’ndende ndi chakudya kapena mowa. Ndamangidwapo nthawi zosawerengeka, koma ndiku- lumbira makate Baibulo, sizinayambepo zachitika kuti anthu ku- mangidwa osasechedwa mokwanira akamalowa muno . . . Nsapato zathu, ndalama komanso zina zonse zimatsala panja. Ndiye lerolo chachitika n’chiyani? Ayi ndithu, kamba anga mwala! Tatifotokozereni bwinobwino chimene chachitika!” Kenako anakhala pansi. Anthu onse anali muselo muja anatembenukira kwa Matigari, ndipo ankayembekezera kuti awauza chinachake chapadera, chifukwa zimene wamowa uja ananena zinali zoona ndithu. Onse anamangidwa patsikulo. Ko- ma palibe amene analandidwa zinthu zake. Ndiyeno Matigari anayamba kuyankhula ngati mmene bambo amayankhulira kwa ana ake. 93