Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 93

Matigari “Limenelo silingakhale vuto, ndikhoza kudya zimene mungasiyezo,” anatero wakuba nsima uja. “Chifukwa chiyani? Kodi nawenso ndi woipa mtima mofanana ndi bambo wa munkhani ija, yemwe anapanirira yek- ha poto wa chakudya mkazi wake woyembekezera akufa ndi njala?” woyendayenda uja anafunsa. “Kapena uli ngati anthu oipa mtima omwe akuyendetsa dziko lino? Ndi mlimi uja yemwe anali ndi yankho la vuto lawoli. “Ndinamangidwa pamene ndimachokera kogula makandu- lo,” anatero. “Tikhoza kuyatsa m'modzi kapena muwiri kuti azitiunikira tikamadya. Ndi njalayidi wina akhoza kupezeka wa- tafunira limodzi ndi chala cha mnzake. Nanga mdima wake umenewu nthuni? Koma vuto ndi lakuti ndilibe machesi.” “Ine ndili nawo,” anatero mphunzitsi uja. Anayatsa makandulo awiri. Kenako anayamba kuyang'anana nkhope ngati akufufuza munthu amene anawapatsa chakudyacho. Pankangooneka zithunzithunzi ndipo zina zinka- onekera pakhoma. Kenako anayamba kuyang'ana Matigari mwachidwi.” Matigari anatenga chakudyacho n'kuchinyemanyema ndipo kenako anawapatsa. Anthuwo anayamba kudya. Kenako anatenga botolo la mowa lija, kulitsegula ndi mano ndipo ke- nako anapungula pang'ono pansi ngati nsembe yoteta mizimu yamakolo. Kenako anapereka botololo kuti aliyense akonkheko kukhosi n’kupereka kwa mnzake. Ndiyeno litafika pa woledzera uja, anaimirira atagwira chakudya chija ndi dzanja limodzi komanso botolo la mowalo ndi dzanja linali ndipo anayamba kuyankhula ngati 92