Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 89

Matigari Wina anamangidwa pamlandu wopha mpondamakwacha wina chifukwa ankalephera kumulipira ndalama yaganyu yo- lima yomwe anagwira. ”Amangondipondetsa moti ndinafika potopa nazo. Ko- mansotu ndinangomumenya ndi ndodo basi, kenako anagwera pansi n'kumwalira . . . zimene amachita zinandikwana. Tangoganizani kunyumba mkazi komanso ana akudikirira kuti upititse ya ufa, koma iwe n'kupitako chimanjamanja. Ndipotu sikuti ndinapita kukapempha. Ndimakatenga ndalama zomwe ndinakhetsera thukuta langa.” Wina anamangidwa chifuka ankangoyendayenda m'tauni. “Kodi anandipatsapo mwayi wantchito? Amangolembana pachibale basi. Tangoganizani kumangidwa chifukwa chopeze- ka ukuyendayenda m'dziko lako lomwe.” Pagululi panalinso wophunzira kusukulu yaukachenjede yemwe anauza mkulu wina waboma kuti zinthu sizikuyenda bwino kungochokera pamene dziko lawo linalandira ufulu wodzilamulira. “Kodi mukudziwa zimene ndinamufunsa? ‘N’chifukwa chi- yani mumavalabe mayunifomu omwe atsamunda ankavala?’ Nanga iwowo ndi milungu kuti tisamawafunse mafunso? Ko d i demokalase ili kuti m'dziko muno? Mkulu wabomayo anaopseza kuti: ‘Muona zokhoma ana a kuyunivesite inu!’ Atanena zimenezi ndiye ndinamumasura. Ndinamuuza kuti, ‘Inuyo, mwalephera kukwaniritsa udindo wanu, nanga chikuchitika n'chiyani m'dzikoli? Kodi nanunso ndi zidole za akuluakulu a boma?’ At- amva zimenezo anakwiya nane n’kunena kuti, ‘Taonani ana osapola panchombo akutukwana anthu akuluakulu!’ Koma ine ndinamuuza kuti kukula si kanthu. Kuona fisi si kubadwa kale. 88